Numeri 7:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. anadza naco copereka cao pamaso pa Yehova, magareta ophimbika asanu ndi mmodzi, ndi ng'ombe khumi ndi ziwfri; akalonga awiri anapereka gareta mmodzi, ndi kalonga mmodzi ng'ombe imodzi; nabwera nazo pakhomo pa kacisi.

4. Ndipo Yehova ananena ndi Mose, ndi kuti,

5. Uzilandira kwa iwo, kuti zikhale zakucitira nchito ya cihema cokomanako; nuzipereke kwa Alevi, yense monga mwa nchito yace.

6. Ndipo Mose analandira magareta ndi ng'ombe, nazipereka kwa Alevi.

7. Anapatsa ana a Gerisoni magareta awiri ndi ng'ombe zinai, monga mwa nchito yao;

Numeri 7