5. Ndipo Yehova anaika mau m'kamwa mwa Balamu, nati, Bwerera kwa Balaki, nukanene cakuti cakuti.
6. Ndipo anabwerera kwa iye, ndipo, taonani, analikuima pa nsembe yopsereza yace, iye ndi akalonga onse a Moabu.
7. Ndipo ananena fanizo lace, nati,Ku Aramu ananditenga Balaki,Mfumu ya Moabu ananditenga ku mapiri a kum'mawa;Idza, udzanditembererere Yakobo.Idza, nudzanyoze Israyeli.
8. Ndidzatemberera bwanji amene Mulungu sanamtemberera?Ndidzanyoza bwanji, amene Yehova sanamnyoza?
9. Pakuti, pokhala pamwamba pa matanthwe ndimpenya,Pokhala pa zitunda ndimuyang'ana;Taonani, ndiwo anthu akukhala paokha.Osadziwerengera pakati pa amitundu ena,
10. Adzawerenga ndani pfumbi la Yakobo,Kapena kuwerenga limodzi la magawo anai la Israyeli?Ndipo ine ndife monga amafa aongoka mtima,Citsiriziro canga cifanane naco cace!