Numeri 2:17-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Pamenepo khamu la Alevi azimuka naco cihema cokomanako, pakati pa makamu; monga amamanga mahema ao, momwemo azimuka ulendo wao, munthu yense pamalo pace, monga mwa mbendera zao.

18. Mbendera ya cigono ca Efraimu izikhala kumadzulo monga mwa makamu ao; ndipo kalonga wa ana a Efraimu ndiye Elisama mwana wa Amihudi.

19. Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi anai kudza mazana asanu.

20. Ndipo oyandikizana naye ndiwo a pfuko la Manase; ndi kalonga wa ana a Manase ndiye Gamaliyeli mwana wa Pedazuri.

21. Ndi khamu lace, ndi owerengedwa ace, ndiwo zikwi makumi atatu mphambu ziwiri kudza mazana awiri.

22. Ndi pfuko la Benjamini: kalonga wa ana a Benjamini ndiye Abidana mwana wa Gideoni.

Numeri 2