33. owerengedwa ao a pfuko la Efraimu, ndiwo zikwi makumi anai mphambu mazana asanu.
34. A ana a Manase, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;
35. owerengedwa ao a pfuko la Manase, ndiwo zikwi makumi atatu mphambu ziwiri kudza mazana awiri.
36. A ana a Benjamini, kubadwa kwao, monga mwa mabanja ao, monga mwa nyumba za makolo ao, powerenga maina, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, onse akuturukira kunkhondo;