Genesis 25:12-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Mibadwo ya Ismayeli mwana wamwamuna wace wa Abrahamu, amene Hagara M-aigupto mdzakazi wa Sara anambalira Abrahamu ndi iyi:

13. ndipo maina a ana a Ismayeli, maina ao m'mibadwo yao ndi awa: woyamba wa Ismayeli ndi Nebayoti; ndi Kedara, ndi Abideele, ndi Mibisamu,

14. ndi Misima, ndi Duma; ndi Masa;

15. ndi Hadada, ndi Tema, ndi Yeturi, ndi Nafisi, ndi Kedema;

16. ana a Ismayeli ndi awa: maina ao m'midzi yao, m'misasa yao ndi awa: akaronga khumi ndi awiri m'mitundu yao.

Genesis 25