Genesis 16:10-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa iye, Ndidzacurukitsa ndithu mbeu zako, kuti unyinji wao sudzawerengeka.

11. Ndipo mthenga wa Yehova anati kwa iye, Taona, uli ndi pakati, ndipo udzabala mwana wamwamuna; nudzamucha dzina lace Ismayeli; cifukwa Yehova anamva kusauka kwako.

12. Ndipo iye adzakhala munthu wa m'thengo; ndipo dzanja lace lidzakhala lotsutsana ndi anthu onse, ndi manja a anthu onse adzakhala otsutsana naye: ndipo iye adzakhala pamaso pa abale ace onse.

Genesis 16