Danieli 6:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Kudamkomera Dariyo kuikira ufumuwo akalonga zana limodzi mphambu makumi awiri akhale m'madera onse a ufumu;

2. ndi akuyang'anira iwo akulu atatu, woyamba wao ndi Danieli; kuti akalonga awa adziwerengere kwa iwo, ndi kuti za mfumu zisasoweke.

3. Pamenepo Danieli amene anaposa akuluwa ndi akalonga, popeza munali mzimu wopambana mwa iye, ndi mfumu inati imuike woyang'anira ufumu wonse.

4. Ndipo akuluwa ndi akalonga anayesa kumtola cifukwa Danieli, kunena za ufumuwo; koma sanakhoza kupeza cifukwa kapena colakwira, popeza anali wokhulupirika; ndipo sanaona cosasamala kapena colakwa ciri conse mwa iye.

5. Pamenepo anthu awa anati, Sitidzamtola cifukwa ciri conse Danieli amene, tikapanda kumtola ici pa cilamulo ca Mulungu wace.

6. Ndipo akuru awa ndi akalonga anasonkhana kwa mfumu mofulumira, natero nayo, Mfumu Dariyo, mukhale ndi moyo cikhalire.

Danieli 6