Danieli 2:33-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

33. miyendo yace yacitsulo, mapazi ace mwina citsulo mwina dongo.

34. Munali cipenyere kufikira mwala unasemedwa popanda manja, umene unagunda fanoli pa mapazi ace okhala citsulo ndi dongo, nuwaphwanya.

35. Pamenepo citsulo, dongo, mkuwa, siliva, ndi golidi, zinapereka pamodzi, nizinasanduka ngati mungu wa pa madwale a malimwe; ndi mphepo inaziuluza, osapezekanso malo ao; ndi mwala udagunda fanowo unasanduka phiri lalikuru, nudzaza dziko lonse lapansi.

36. Ili ndi loto; kumasulira kwace tsono tikufotokozerani mfumu.

Danieli 2