40. Ndipo nthawi yotsiriza mfumu ya kumwela idzalimbana naye, ndi mfumu ya kumpoto idzamdzera ngati kabvumvulu, ndi magareta, ndi apakavalo, ndi zombo zambiri; nadzalowa m'maiko, nadzasefukira ndi kupitirira.
41. Adzalowanso m'dziko lokometsetsalo ndi maiko ambiri adzapasuka; koma opulumuka dzanja lace ndi awa: Edomu, ndi Moabu, ndi oyamba a ana a Amoni.
42. Adzatambalitsiranso dzanja lace kumaiko; dziko la Aigupto lomwe silidzapulumuka.
43. Ndipo adzacita mwamphamvu ndi cuma ca golidi, ndi siliva, ndi zinthu zofunika zonse za Aigupto; Alubi ndi Akusi adzatsata mapazi ace.