6. Mwa awa tsono munali a ana a Yuda, Danieli, Hananiya, Misayeli, ndi Azariya.
7. Ndi mkuru wa adindo anawapatsa maina ena; Danieli anamucha Belitsazara; ndi Hananiya, Sadrake; ndi Misaeli, Mesaki; ndi Azariya, Abedinego.
8. Koma Danieli anatsimikiza mtimti kuti asadzidetse ndi cakudya ca mfumu, kapena ndi vinyo amamwa; cifukwa cace anapempha mkuru wa adindo amlole asadzidetse.
9. Ndipo Mulungu anamkometsera Danieli mtima wa mkuru wa adindo, amcitire cifundo.