Cibvumbulutso 9:5-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo anapatsa ilo mphamvu si kuti likawaphe, komatu kuti likawazunze miyezi isanu; ndipo mazunzidwe ao anali ngati mazunzidwe a cinkhanira, pamene ciluma munthu.

6. Ndipo m'masiku ajawo, anthu adzafunafuna imfa osaipeza konse; ndipo adzakhumba kumwalira, koma imfa idzawathawa.

7. Ndipo maonekedwe a dzombelo anafanana ndi akavalo okonzeka kukacita nkhondo; ndi pamitu pao ngati akorona onga agolidi, ndi pankhope pao ngati pankhope pa anthu.

8. Ndipo anali nalo tsitsi Ionga tsitsi la akazi, ndipo mano ao analingati mano a mikango.

9. Ndipo anali nazo zikopa ngati zikopa zacitsulo; ndipo mkokomo wa: mapiko ao ngati mkokomo wa agareta, a akavalo ambiri akuthamangira kunkhondo.

10. Ndipo liri nayo micira yofanana ndi ya cinkhanira ndi mbola; ndipo m'micira mwao muli mphamvu yao yakuipsa anthu miyezi isanu.

11. Ndipo linali nayo Mfumu yakulilamulira, mngelo wa phompho; dzina lace m'Cihebri Abadoni, ndi m'Cihelene ali nalo dzina Apoliyoni.

12. Tsoka loyamba lapita; taonani, akudzanso masoka awiri m'tsogolomo.

13. Ndipo mngelo wacisanu ndi cimodzi anaomba, ndipo ndinamva mau ocokera ku nyanga za guwa la nsembe lagolidi liri pamaso pa Mulungu,

Cibvumbulutso 9