13. ndipo pakati pa zoikapo nyalizo wina wonga Mwana wa munthu atabvala cobvala cofikira ku mapazi ace, atamangira lamba lagolidi pacifuwa.
14. Ndipo tsitsi la pamutu pace linali loyera ngati ubweya woyera, ngati cipale cofewa; ndi maso ace ngati lawi la moto;
15. ndi mapazi ace ngati mkuwa wonyezimira, ngati woyengeka m'ng'anjo; ndi mau ace ngati mkokomo wa madzi ambiri.