Ahebri 5:7-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ameneyo, m'masiku a thupi lace anapereka mapemphero ndi mapembedzero pamodzi ndi kulira kwakukuru ndi misozi kwa iye amene anakhoza kumpulumutsa iye muimfa, ndipo anamveka popeza anaopa Mulungu,

8. angakhale anali Mwana, anaphunzira kumvera ndi izi adamva kuwawa nazo;

9. ndipo pamene anakonzeka wamphumphu anakhala kwa onse akumvera iye cifukwa ca cipulumutso cosatha;

Ahebri 5